(en chichewa)

Mlungu dalitsani Malawi,
Mumsunge m'mtendere.
Gonjetsani adani onse,
Njala, nthenda, nsanje.
Lunzitsani mitima yathu,
Kuti tisaope.
Mdalitse Mtsogo leri nafe,
Ndi Mai Malawi.

  

Malawi ndziko lokongola,
La chonde ndi ufulu,
Nyanja ndi mphepo ya m'mapiri,
Ndithudi tadala.
Zigwa, mapiri, nthaka, dzinthu,
N'mphatso zaulere.
Nkhalango, madambo abwino.
Ngwokoma Malawi.

  

O Ufulu tigwirizane,
Kukweza Malawi.
Ndi chikondi, khama, kumvera,
Timutumikire.
Pa nkhondo nkana pa mtendere,
Cholinga n'chimodzi.
Mai, bambo, tidzipereke,
Pokweza Malawi.

  

  

  

  

  

  

  

  

  

|  En chichewa   

|  En inglés         

|  En español      

  

  

  

  

  

  

  

  

 

Himno de
MALAUI
     
Letra y Música:
Michael - Frederick Paul Sauka

Año: 1964 (adoptado)
 

  Datos    Bandera    Mapa